Settings
Surah Quraish [Quraish] in Chewa
Surah Quraish [Quraish] Ayah 4 Location Makkah Number 106
لِإِیلَـٰفِ قُرَیۡشٍ ﴿1﴾
Cholinga chakuwachita Maquraish kuti apitirize chizolowezi chawo,[486]
إِۦلَـٰفِهِمۡ رِحۡلَةَ ٱلشِّتَاۤءِ وَٱلصَّیۡفِ ﴿2﴾
Apitilize chizolowezi chawo choyenda nthawi ya dzinja (kunka ku Yemen) ndi nthawi yachirimwe (kunka ku Sham kukachita malonda, mosatekeseka ndi mopanda mantha).
فَلۡیَعۡبُدُوا۟ رَبَّ هَـٰذَا ٱلۡبَیۡتِ ﴿3﴾
Choncho, amupembedze Mbuye wa Nyumba iyi (Al-Kaaba amene adachititsa kuti athe kuyenda maulendo awiriwo).
ٱلَّذِیۤ أَطۡعَمَهُم مِّن جُوعࣲ وَءَامَنَهُم مِّنۡ خَوۡفِۭ ﴿4﴾
Yemwe amawadyetsa (nthawi imene Arabu anzawo) ali m’njala, ndipo amawapatsa chitetezo (pomwe anzawo) ali ndi mantha.