Main pages

Surah Alms Giving [Al-Maun] in Chewa

Surah Alms Giving [Al-Maun] Ayah 7 Location Makkah Number 107

أَرَءَيْتَ ٱلَّذِى يُكَذِّبُ بِٱلدِّينِ ﴿1﴾

Kodi wamuona yemwe akutsutsa za mphoto (ndi chiwerengero cha tsiku lachimaliziro)?[487]

فَذَٰلِكَ ٱلَّذِى يَدُعُّ ٱلْيَتِيمَ ﴿2﴾

Iye ndi yemwe akukankha wamasiye (mwankhanza).

وَلَا يَحُضُّ عَلَىٰ طَعَامِ ٱلْمِسْكِينِ ﴿3﴾

Ndipo salimbikitsa (ena pamodzi ndi iye mwini) kudyetsa osauka.

فَوَيْلٌۭ لِّلْمُصَلِّينَ ﴿4﴾

Choncho kuonongeka kuli pa ena mwa opemphera swala (amene ali ndi mbiri izi);

ٱلَّذِينَ هُمْ عَن صَلَاتِهِمْ سَاهُونَ ﴿5﴾

Omwe amachitira mphwayi mapemphero awo.[488]

ٱلَّذِينَ هُمْ يُرَآءُونَ ﴿6﴾

Amenenso (akamachita mapemphero awo) amadzionetsera (kwa anthu mwachipha maso kuti apeze ulemelero ndi kutamandidwa mmitima mwa anthu).[489]

وَيَمْنَعُونَ ٱلْمَاعُونَ ﴿7﴾

Ndipo amamana ziwiya (zawo posabwereka anzawo zinthu zofunika pa moyo wa aliyense monga nkhwangwa, mpeni, mtondo ndi zina zotere).