Main pages

Surah The Disbelievers [Al-Kafiroon] in Chewa

Surah The Disbelievers [Al-Kafiroon] Ayah 6 Location Makkah Number 109

قُلۡ یَـٰۤأَیُّهَا ٱلۡكَـٰفِرُونَ ﴿1﴾

Nena (iwe Mtumiki) (s.a.w): E inu anthu osakhulupirira![493]

لَاۤ أَعۡبُدُ مَا تَعۡبُدُونَ ﴿2﴾

Sindipembedza chimene inu mukuchipembedza (kusiya Allah).

وَلَاۤ أَنتُمۡ عَـٰبِدُونَ مَاۤ أَعۡبُدُ ﴿3﴾

Inunso simumpembedza amene ine ndikumpembedza (yemwe ndi Allah).

وَلَاۤ أَنَا۠ عَابِدࣱ مَّا عَبَدتُّمۡ ﴿4﴾

Ndiponso ine sindidzapembedza chimene inu mwakhala mukuchipembedza (chifukwa inu ndinu ophatikiza Allah ndi zinthu zina).

وَلَاۤ أَنتُمۡ عَـٰبِدُونَ مَاۤ أَعۡبُدُ ﴿5﴾

Ndipo inu simudzampembedza amene ine ndikumpembedza (yemwe ndi Allah).

لَكُمۡ دِینُكُمۡ وَلِیَ دِینِ ﴿6﴾

Inu muli ndi chipembedzo chanu (chimene mukuchikhulupirira), inenso ndili ndi chipembedzo changa (chimene Allah wandisankhira).