Settings
Surah The Flame [Al-Masadd] in Chewa
تَبَّتْ يَدَآ أَبِى لَهَبٍۢ وَتَبَّ ﴿1﴾
Aonongeka manja a Abi Lahab (omwe adali kuwagwiritsa ntchito pozunza Asilamu). Nayenso wawonongeka.[497]
مَآ أَغْنَىٰ عَنْهُ مَالُهُۥ وَمَا كَسَبَ ﴿2﴾
Chuma chake ndi ulemelero wake (umene adaupeza) sizidamthandize ku chilango cha Allah.
سَيَصْلَىٰ نَارًۭا ذَاتَ لَهَبٍۢ ﴿3﴾
Adzalowa ku Moto wa malawi.
وَٱمْرَأَتُهُۥ حَمَّالَةَ ٱلْحَطَبِ ﴿4﴾
Nayenso mkazi wake (adzalowa ku Moto) yemwe adali kusenza nkhuni (za minga pomutchera Mtumiki (s.a.w) komanso amanka nadanitsa pakati pa anthu).
فِى جِيدِهَا حَبْلٌۭ مِّن مَّسَدٍۭ ﴿5﴾
Mkhosi mwake mdzamangidwa chingwe chopiringidwa bwino cha mlaza (chomlanga nacho).[498]