Main pages

Surah The tidings [An-Naba] in Chewa

Surah The tidings [An-Naba] Ayah 40 Location Makkah Number 78

عَمَّ يَتَسَآءَلُونَ ﴿1﴾

۞ Kodi akufunsana zachiyani?

عَنِ ٱلنَّبَإِ ٱلْعَظِيمِ ﴿2﴾

Za nkhani yayikulu ija.

ٱلَّذِى هُمْ فِيهِ مُخْتَلِفُونَ ﴿3﴾

Imene iwo akusiyana (maganizo).[372]

كَلَّا سَيَعْلَمُونَ ﴿4﴾

Aleke (zimenezo) adzadziwa posachedwapa.[373]

ثُمَّ كَلَّا سَيَعْلَمُونَ ﴿5﴾

Ayi, ndithu aleke (zimenezo); posachedwapa adzadziwa zoona zake (pamene chilango chidzawatsikira).[374]

أَلَمْ نَجْعَلِ ٱلْأَرْضَ مِهَٰدًۭا ﴿6﴾

Kodi sitidachite nthaka kukhala ngati choyala?[375]

وَٱلْجِبَالَ أَوْتَادًۭا ﴿7﴾

Ndi mapiri ngati zichiri (zolimbitsa nthaka)?

وَخَلَقْنَٰكُمْ أَزْوَٰجًۭا ﴿8﴾

Ndipo takulengani mitundu iwiri (amuna ndi akazi).

وَجَعَلْنَا نَوْمَكُمْ سُبَاتًۭا ﴿9﴾

Ndipo tidachita tulo tanu kukhala mpumulo (ku mavuto a ntchito).

وَجَعَلْنَا ٱلَّيْلَ لِبَاسًۭا ﴿10﴾

Ndipo taupanga usiku kukhala ngati chovala (pokuvindikirani ndi mdima wake).

وَجَعَلْنَا ٱلنَّهَارَ مَعَاشًۭا ﴿11﴾

Ndipo tapanga masana kukhala nthawi yopezera zofunika pa moyo;

وَبَنَيْنَا فَوْقَكُمْ سَبْعًۭا شِدَادًۭا ﴿12﴾

Ndipo tamanga pamwamba panu thambo zisanu ndi ziwiri zolimba;

وَجَعَلْنَا سِرَاجًۭا وَهَّاجًۭا ﴿13﴾

Ndipo tidapanga nyali yowala ndi yotentha kwambiri (dzuwa);

وَأَنزَلْنَا مِنَ ٱلْمُعْصِرَٰتِ مَآءًۭ ثَجَّاجًۭا ﴿14﴾

Ndipo tawatsitsa madzi otsika mwamphamvu kuchokera ku mitambo, ya mvula;

لِّنُخْرِجَ بِهِۦ حَبًّۭا وَنَبَاتًۭا ﴿15﴾

Kuti titulutse ndi madziwo mbewu ndi m’mera, (chomwe ndi chakudya cha anthu ndi nyama).

وَجَنَّٰتٍ أَلْفَافًا ﴿16﴾

Ndi minda yothothana nthambi za mitengo.

إِنَّ يَوْمَ ٱلْفَصْلِ كَانَ مِيقَٰتًۭا ﴿17﴾

Ndithu tsiku la chiweruziro ndinthawi imene idakhazikitsidwa kale.

يَوْمَ يُنفَخُ فِى ٱلصُّورِ فَتَأْتُونَ أَفْوَاجًۭا ﴿18﴾

Tsiku limene lipenga (lakuuka) lidzaimbidwa ndipo inu mudzabwera (kubwalo losonkhanirana) muli magulumagulu.

وَفُتِحَتِ ٱلسَّمَآءُ فَكَانَتْ أَبْوَٰبًۭا ﴿19﴾

Ndipo thambo lidzatsegulidwa (mbali zonse): choncho lidzakhala makomomakomo.

وَسُيِّرَتِ ٱلْجِبَالُ فَكَانَتْ سَرَابًا ﴿20﴾

Ndipo mapiri adzachotsedwa m’malo mwake, adzakhala ngati zideruderu.[376]

إِنَّ جَهَنَّمَ كَانَتْ مِرْصَادًۭا ﴿21﴾

Ndithu moto wa Jahannam ukuwadikilira (oipa).

لِّلطَّٰغِينَ مَـَٔابًۭا ﴿22﴾

Mbuto ya opyola malire.[377]

لَّٰبِثِينَ فِيهَآ أَحْقَابًۭا ﴿23﴾

Adzakhala m’menemo muyaya.

لَّا يَذُوقُونَ فِيهَا بَرْدًۭا وَلَا شَرَابًا ﴿24﴾

Sadzalawa m’menemo kuzizira (kowachotsera kutentha), kapena chakumwa (chowachotsera ludzu lawo);

إِلَّا حَمِيمًۭا وَغَسَّاقًۭا ﴿25﴾

Kupatula madzi otentha kwambiri ndi mafinya (otuluka mmatupi a anthu a ku Moto);

جَزَآءًۭ وِفَاقًا ﴿26﴾

Kukhala malipiro olingana ndi ntchito zawo.

إِنَّهُمْ كَانُوا۟ لَا يَرْجُونَ حِسَابًۭا ﴿27﴾

Ndithu iwo sadali kuyembekezera chiwerengero (cha Allah);

وَكَذَّبُوا۟ بِـَٔايَٰتِنَا كِذَّابًۭا ﴿28﴾

Adatsutsa zizindikiro Zathu (zosonyeza kuuka kwa akufa) ndi mtsutso waukulu.

وَكُلَّ شَىْءٍ أَحْصَيْنَٰهُ كِتَٰبًۭا ﴿29﴾

Ndipo chinthu chilichonse tachisunga mochilemba.

فَذُوقُوا۟ فَلَن نَّزِيدَكُمْ إِلَّا عَذَابًا ﴿30﴾

Basi, lawani (lero chilango Changa); sitikuonjezerani chinthu china koma chilango pamwamba pa chilango.

إِنَّ لِلْمُتَّقِينَ مَفَازًا ﴿31﴾

Ndithu anthu oopa Allah adzakhala ndi malo wopambana.

حَدَآئِقَ وَأَعْنَٰبًۭا ﴿32﴾

Minda ndi zipatso za mphesa.

وَكَوَاعِبَ أَتْرَابًۭا ﴿33﴾

Ndi mabuthu (anamwali) ofanana misinkhu.

وَكَأْسًۭا دِهَاقًۭا ﴿34﴾

Ndi zipanda zodzaza ndi zakumwa.

لَّا يَسْمَعُونَ فِيهَا لَغْوًۭا وَلَا كِذَّٰبًۭا ﴿35﴾

Sakamva m’menemo mawu opanda pake kapena bodza.

جَزَآءًۭ مِّن رَّبِّكَ عَطَآءً حِسَابًۭا ﴿36﴾

Amenewa ndi malipiro ochokera kwa Mbuye wako zopereka zokwanira.[378]

رَّبِّ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلْأَرْضِ وَمَا بَيْنَهُمَا ٱلرَّحْمَٰنِ ۖ لَا يَمْلِكُونَ مِنْهُ خِطَابًۭا ﴿37﴾

Mbuye wa kumwamba ndi pansi ndi zimene zili pakati pake; Wachifundo chambiri. Palibe amene adzakhala ndi mphamvu yolankhulana naye (pa tsiku limenero);

يَوْمَ يَقُومُ ٱلرُّوحُ وَٱلْمَلَٰٓئِكَةُ صَفًّۭا ۖ لَّا يَتَكَلَّمُونَ إِلَّا مَنْ أَذِنَ لَهُ ٱلرَّحْمَٰنُ وَقَالَ صَوَابًۭا ﴿38﴾

Tsiku limene adzaima Jibril ndi angelo pa mzere (ali odzichepetsa); sadzayankhula aliyense mwa iwo kupatula yekhayo amene adzaloledwa ndi (Allah) Wachifundo chambiri (kuyankhula) ndipo adzanena zolondola.

ذَٰلِكَ ٱلْيَوْمُ ٱلْحَقُّ ۖ فَمَن شَآءَ ٱتَّخَذَ إِلَىٰ رَبِّهِۦ مَـَٔابًا ﴿39﴾

Limenelo ndi tsiku loona, (lopanda chikaiko); choncho amene akufuna adzipezere malo (njira yonkera) kwa Mbuye wake. (Pomugonjera Iye pa moyo uno wadziko lapansi).

إِنَّآ أَنذَرْنَٰكُمْ عَذَابًۭا قَرِيبًۭا يَوْمَ يَنظُرُ ٱلْمَرْءُ مَا قَدَّمَتْ يَدَاهُ وَيَقُولُ ٱلْكَافِرُ يَٰلَيْتَنِى كُنتُ تُرَٰبًۢا ﴿40﴾

Ndithu tikukuchenjezani zachilango chomwe chili pafupi kudza; tsiku limene munthu adzayang’ana zimene adatsogoza manja ake, ndipo wosakhulupirira adzanena: Kalanga ine! Ndikadakhala dothi, (kuti ndisalangidwe chilango chikundiyembekezachi).