Main pages

Surah The Sundering, Splitting Open [Al-Inshiqaq] in Chewa

Surah The Sundering, Splitting Open [Al-Inshiqaq] Ayah 25 Location Makkah Number 84

إِذَا ٱلسَّمَآءُ ٱنشَقَّتْ ﴿1﴾

Pamene thambo lidzang’ambike (kusonyeza mapeto ake),

وَأَذِنَتْ لِرَبِّهَا وَحُقَّتْ ﴿2﴾

Ndikudzamvera lamulo la Mbuye wake; ndipo lidzayenera kutero,

وَإِذَا ٱلْأَرْضُ مُدَّتْ ﴿3﴾

Ndiponso pamene nthaka idzatambasulidwe (pogumuka mapiri ake ndikuchoka zitunda zake),

وَأَلْقَتْ مَا فِيهَا وَتَخَلَّتْ ﴿4﴾

Ndi kutaya zomwe zidali mkati mwake ndi kukhala yopanda kanthu,[405]

وَأَذِنَتْ لِرَبِّهَا وَحُقَّتْ ﴿5﴾

Ndikudzamvera lamulo la Mbuye wake; ndipo lidzayenera kutero. (Choncho zikadzachitika zimenezi ndiye kuti munthu adzalandira mphoto ya zochita zake).[406]

يَٰٓأَيُّهَا ٱلْإِنسَٰنُ إِنَّكَ كَادِحٌ إِلَىٰ رَبِّكَ كَدْحًۭا فَمُلَٰقِيهِ ﴿6﴾

E iwe munthu! Ndithudi iwe ukubwerera kwa Mbuye wako (ndi zochita zako zabwino kapena zoipa), kubwerera kotsimikizika, ndipo iwe ukumana (ndi zotsatira za zochitachita zako).

فَأَمَّا مَنْ أُوتِىَ كِتَٰبَهُۥ بِيَمِينِهِۦ ﴿7﴾

Tsono amene adzapatsidwe kaundula wa zochita zake kudzanja la manja,[407]

فَسَوْفَ يُحَاسَبُ حِسَابًۭا يَسِيرًۭا ﴿8﴾

Basi iye, adzawerengedwa, kuwerengedwa kopepuka,[408]

وَيَنقَلِبُ إِلَىٰٓ أَهْلِهِۦ مَسْرُورًۭا ﴿9﴾

Ndipo adzabwerera kwa anthu ake (okhulupirira) ali wokondwa.

وَأَمَّا مَنْ أُوتِىَ كِتَٰبَهُۥ وَرَآءَ ظَهْرِهِۦ ﴿10﴾

Koma yemwe adzapatsidwe kaundula wa zochita zake chakumanzere kudzera kumbuyo kwa msana wake (chifukwa chomunyoza),

فَسَوْفَ يَدْعُوا۟ ثُبُورًۭا ﴿11﴾

Basi, iye adzaitana imfa (kuti imufikire; kuti afe apumule, koma siidzamufikira);

وَيَصْلَىٰ سَعِيرًا ﴿12﴾

Ndipo adzalowa ku Moto woyaka.

إِنَّهُۥ كَانَ فِىٓ أَهْلِهِۦ مَسْرُورًا ﴿13﴾

Kamba kakuti iye adali wokondwa; (kukondwa kwa machimo) pamodzi ndi anthu ake (osaganizira za mathero ake).

إِنَّهُۥ ظَنَّ أَن لَّن يَحُورَ ﴿14﴾

Ndithudi, amaganiza kuti sadzabwerera (kwa Allah ndiponso sadzawerengedwa).

بَلَىٰٓ إِنَّ رَبَّهُۥ كَانَ بِهِۦ بَصِيرًۭا ﴿15﴾

Chifukwa ninji (asabwelere)? Ndithu Mbuye wake adali kumuona. (Choncho alipidwa zimene adachita).

فَلَآ أُقْسِمُ بِٱلشَّفَقِ ﴿16﴾

Choncho ndikulumbilira kufiira kwa dzuwa (pamene likulowa).

وَٱلَّيْلِ وَمَا وَسَقَ ﴿17﴾

Ndi usiku ndi zimene wasonkhanitsa,[409]

وَٱلْقَمَرِ إِذَا ٱتَّسَقَ ﴿18﴾

Ndi mwezi ukakwanira dangalira (lake),

لَتَرْكَبُنَّ طَبَقًا عَن طَبَقٍۢ ﴿19﴾

Ndithudi mudzachoka apa kunka apa (pa moyo uno mpakana umene uli nkudza).

فَمَا لَهُمْ لَا يُؤْمِنُونَ ﴿20﴾

Kodi nchiyani chikuwaletsa iwo (okanira) kukhulupirira (Allah ndi kuuka kumanda, zisonyezo zake zitaonekera poyera)?

وَإِذَا قُرِئَ عَلَيْهِمُ ٱلْقُرْءَانُ لَا يَسْجُدُونَ ۩ ﴿21﴾

Ndipo ikawerengedwa kwa iwo Qur’an, sagwetsa pansi nkhope zawo (modzichepetsa).

بَلِ ٱلَّذِينَ كَفَرُوا۟ يُكَذِّبُونَ ﴿22﴾

Koma amene sadakhulupirire akutsutsa basi (chifukwa cha makani ndi kudzikweza).

وَٱللَّهُ أَعْلَمُ بِمَا يُوعُونَ ﴿23﴾

Ndipo Allah akudziwa (bwinobwino) zimene akuzisonkhanitsa.

فَبَشِّرْهُم بِعَذَابٍ أَلِيمٍ ﴿24﴾

Choncho, auze nkhani yachilango chopweteka.

إِلَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوا۟ وَعَمِلُوا۟ ٱلصَّٰلِحَٰتِ لَهُمْ أَجْرٌ غَيْرُ مَمْنُونٍۭ ﴿25﴾

Kupatula awo amene akhulupirira ndikuchita ntchito zabwino, kwa iwo kuli malipiro osatha.[410]