Settings
Surah The Most High [Al-Ala] in Chewa
سَبِّحِ ٱسْمَ رَبِّكَ ٱلْأَعْلَى ﴿1﴾
Lemekeza dzina la Mbuye wako Wapamwambamwamba (ndikuliyeretsa ku zinthu zosayenera).[417]
ٱلَّذِى خَلَقَ فَسَوَّىٰ ﴿2﴾
Amene adalenga (chilichonse) ndikuchikonza bwinobwino (mkalengedwe kolingana).
وَٱلَّذِى قَدَّرَ فَهَدَىٰ ﴿3﴾
Amene adalamuliratu (chilichonse zochita zake) ndi kuchiongolera.[418]
وَٱلَّذِىٓ أَخْرَجَ ٱلْمَرْعَىٰ ﴿4﴾
Ndi Yemwenso akumeretsa msipu.
فَجَعَلَهُۥ غُثَآءً أَحْوَىٰ ﴿5﴾
Ndipo nausandutsa kukhala wouma ndi wodera.
سَنُقْرِئُكَ فَلَا تَنسَىٰٓ ﴿6﴾
Tikulakatulira (chivumbulutso Chathu) ndipo siuyiwala.[419]
إِلَّا مَا شَآءَ ٱللَّهُ ۚ إِنَّهُۥ يَعْلَمُ ٱلْجَهْرَ وَمَا يَخْفَىٰ ﴿7﴾
Kupatula chimene wafuna Allah (kuti uchiiwale); ndithu Iye amadziwa zoonekera ndi zimene zimabisika.
وَنُيَسِّرُكَ لِلْيُسْرَىٰ ﴿8﴾
Ndipo tikufewetsera (njira yochitira zinthu) zabwino.[420]
فَذَكِّرْ إِن نَّفَعَتِ ٱلذِّكْرَىٰ ﴿9﴾
Choncho akumbutse (wanthu powalalikira) ngati kukumbutsa kuthandiza.[421]
سَيَذَّكَّرُ مَن يَخْشَىٰ ﴿10﴾
(Palibe chikaiko ulalikiwo) aukumbukira (ndikuthandizidwa nawo) amene akuopa Allah.
وَيَتَجَنَّبُهَا ٱلْأَشْقَى ﴿11﴾
Ndipo wamavuto ambiri, (wamakani ndi wokanira), adzitalikitsa ndi ulalikiwo.[422]
ٱلَّذِى يَصْلَى ٱلنَّارَ ٱلْكُبْرَىٰ ﴿12﴾
Amene adzalowa ku moto waukulu (umene wakonzedwa kuti udzakhale malipiro ake).
ثُمَّ لَا يَمُوتُ فِيهَا وَلَا يَحْيَىٰ ﴿13﴾
Ndipo sakafa m’menemo (ndikupumula kumazunzo), ndiponso sakakhala ndi moyo (wamtendere).
قَدْ أَفْلَحَ مَن تَزَكَّىٰ ﴿14﴾
Ndithu wapambana amene wadziyeretsa (ku machimo),[423]
وَذَكَرَ ٱسْمَ رَبِّهِۦ فَصَلَّىٰ ﴿15﴾
Ndikukumbukira dzina la Mbuye wake (ndi mtima wake, ndi lirime lake) uku akumapemphera.
بَلْ تُؤْثِرُونَ ٱلْحَيَوٰةَ ٱلدُّنْيَا ﴿16﴾
Koma inu mukukonda kwambiri moyo wa dziko lapansi.
وَٱلْءَاخِرَةُ خَيْرٌۭ وَأَبْقَىٰٓ ﴿17﴾
Pamene moyo wa tsiku lachimaliziro ndiwabwino kwambiri ndiponso wamuyaya.
إِنَّ هَٰذَا لَفِى ٱلصُّحُفِ ٱلْأُولَىٰ ﴿18﴾
Ndithu izi (mukuuzidwa m’Qur’an) zilipo m’mabuku oyamba, akale,[424]
صُحُفِ إِبْرَٰهِيمَ وَمُوسَىٰ ﴿19﴾
Mabuku a Ibrahim ndi Mûsa.