Settings
Surah The night [Al-Lail] in Chewa
وَٱلَّيْلِ إِذَا يَغْشَىٰ ﴿1﴾
Ndikulumbilira usiku pamene ukuphimba (chilichonse).
وَٱلنَّهَارِ إِذَا تَجَلَّىٰ ﴿2﴾
Ndi usana pamene kukuyera.
وَمَا خَلَقَ ٱلذَّكَرَ وَٱلْأُنثَىٰٓ ﴿3﴾
Ndiponso Yemwe adalenga chachimuna ndi chachikazi.
إِنَّ سَعْيَكُمْ لَشَتَّىٰ ﴿4﴾
Ndithu zochita zanu nzosiyanasiyana.[446]
فَأَمَّا مَنْ أَعْطَىٰ وَٱتَّقَىٰ ﴿5﴾
Tsono yemwe akupereka (pa njira ya Allah) ndikumamuopa (Mbuye wake ndikupewa zoletsedwa),[447]
وَصَدَّقَ بِٱلْحُسْنَىٰ ﴿6﴾
Ndikumavomereza zinthu zabwino; (komwe kuli kukhulupirira Allah mwanzeru),[448]
فَسَنُيَسِّرُهُۥ لِلْيُسْرَىٰ ﴿7﴾
Choncho timufewetsera njira yompititsa ku zabwino.[449]
وَأَمَّا مَنۢ بَخِلَ وَٱسْتَغْنَىٰ ﴿8﴾
Koma uyo achite umbombo ndikuganiza za kuti iye payekha ngokwana;
وَكَذَّبَ بِٱلْحُسْنَىٰ ﴿9﴾
Ndi kumatsutsa zinthu zabwino,
فَسَنُيَسِّرُهُۥ لِلْعُسْرَىٰ ﴿10﴾
Choncho timufewetsera njira yompititsa ku mavuto (a muyaya).
وَمَا يُغْنِى عَنْهُ مَالُهُۥٓ إِذَا تَرَدَّىٰٓ ﴿11﴾
Ndipo chuma chake sichidzamthandiza (chilichonse) akadzagwera ku Moto.
إِنَّ عَلَيْنَا لَلْهُدَىٰ ﴿12﴾
Ndithu Ife ndi amene timawalongosolera anthu njira yabwino ndi njira yoipa.
وَإِنَّ لَنَا لَلْءَاخِرَةَ وَٱلْأُولَىٰ ﴿13﴾
Ndipo ndithu moyo womaliza ndi moyo woyamba uli m’manja mwathu.
فَأَنذَرْتُكُمْ نَارًۭا تَلَظَّىٰ ﴿14﴾
Basi, ndikukuchenjezani za Moto woyaka mwa mphamvu.
لَا يَصْلَىٰهَآ إِلَّا ٱلْأَشْقَى ﴿15﴾
Sakaulowa koma (kafiri) woipitsitsa kwambiri.
ٱلَّذِى كَذَّبَ وَتَوَلَّىٰ ﴿16﴾
Yemwe amatsutsa (choona) ndi kunyoza (zisonyezo za Allah).
وَسَيُجَنَّبُهَا ٱلْأَتْقَى ﴿17﴾
Koma yemwe akuopa Allah kwambiri akatalikitsidwa ndi Moto.
ٱلَّذِى يُؤْتِى مَالَهُۥ يَتَزَكَّىٰ ﴿18﴾
Amene akupereka chuma chake ndi cholinga chodziyeretsa.
وَمَا لِأَحَدٍ عِندَهُۥ مِن نِّعْمَةٍۢ تُجْزَىٰٓ ﴿19﴾
Ndipo palibe aliyense kwa iye, amene adamchitira za chifundo zomwe zikulipidwa.[450]
إِلَّا ٱبْتِغَآءَ وَجْهِ رَبِّهِ ٱلْأَعْلَىٰ ﴿20﴾
Koma (akuchita zimenezi) kufuna chikondi cha Mbuye wake Wapamwambamwamba.
وَلَسَوْفَ يَرْضَىٰ ﴿21﴾
Ndipo posachedwa adzasangalala.[451]