Settings
Surah The morning hours [Ad-Dhuha] in Chewa
وَٱلضُّحَىٰ ﴿1﴾
Ndikulumbilira mmawa dzuwa litakwera (imene ili nthawi yantchito),
وَٱلَّيْلِ إِذَا سَجَىٰ ﴿2﴾
Ndi usiku pamene ukuvindikira.
مَا وَدَّعَكَ رَبُّكَ وَمَا قَلَىٰ ﴿3﴾
Sadakusiye Mbuye wako (iwe Mneneri) (s.a.w) ndiponso sadakude.[452]
وَلَلْءَاخِرَةُ خَيْرٌۭ لَّكَ مِنَ ٱلْأُولَىٰ ﴿4﴾
Ndithu moyo watsiku lirimkudza ndi wabwino kwa iwe kuposa umoyo woyambawu.
وَلَسَوْفَ يُعْطِيكَ رَبُّكَ فَتَرْضَىٰٓ ﴿5﴾
Ndithu posachedwapa akupatsa Mbuye wako (zabwino zamdziko lapansi ndi tsiku lachimaliziro) ndipo ukondwera.[453]
أَلَمْ يَجِدْكَ يَتِيمًۭا فَـَٔاوَىٰ ﴿6﴾
Kodi sadakupeze uli wa masiye ndipo adakupatsa pokhala pabwino?
وَوَجَدَكَ ضَآلًّۭا فَهَدَىٰ ﴿7﴾
Ndipo adakupeza uli wosazindikira (Qur’an) nakuongola (pokuzindikiritsa Qur’aniyo ndi malamulo a chipembedzo)?[454]
وَوَجَدَكَ عَآئِلًۭا فَأَغْنَىٰ ﴿8﴾
Ndiponso adakupeza uli wosauka nakulemeretsa?
فَأَمَّا ٱلْيَتِيمَ فَلَا تَقْهَرْ ﴿9﴾
Basi, wamasiye usamchitire nkhanza.
وَأَمَّا ٱلسَّآئِلَ فَلَا تَنْهَرْ ﴿10﴾
Ndiponso wopempha usamukalipire.
وَأَمَّا بِنِعْمَةِ رَبِّكَ فَحَدِّثْ ﴿11﴾
Tsono mtendere wa Mbuye wako uwutchule (pothokoza ndi kugwira ntchito zabwino).