Settings
Surah Solace [Al-Inshirah] in Chewa
أَلَمْ نَشْرَحْ لَكَ صَدْرَكَ ﴿1﴾
Kodi sitidachiphanule chifuwa chako (pokupatsa chiongoko ndi chikhulupiliro ndi nzeru zambiri)?
وَوَضَعْنَا عَنكَ وِزْرَكَ ﴿2﴾
Ndipo takuchotsera mtolo wako (pa ntchito yolalikira pokuthandiza ndi kukufewetsera zinthu zako).
ٱلَّذِىٓ أَنقَضَ ظَهْرَكَ ﴿3﴾
Mtolo umene udalemetsa msana wako?
وَرَفَعْنَا لَكَ ذِكْرَكَ ﴿4﴾
Ndipo takukweza kutchulidwa kwako.[455]
فَإِنَّ مَعَ ٱلْعُسْرِ يُسْرًا ﴿5﴾
Ndipo ndithu pali chovuta palinso zabwino (Zambiri).
إِنَّ مَعَ ٱلْعُسْرِ يُسْرًۭا ﴿6﴾
Ndithu pali chovuta palinso zabwino (zambiri).
فَإِذَا فَرَغْتَ فَٱنصَبْ ﴿7﴾
Basi, ukamaliza ntchito (yolalikira ndi Jihâd) limbikira kupemphera.[456]
وَإِلَىٰ رَبِّكَ فَٱرْغَب ﴿8﴾
Ndipo khala wolakalaka (zabwino zomwe zili) kwa Mbuye wako.