Main pages

Surah The Clot [Al-Alaq] in Chewa

Surah The Clot [Al-Alaq] Ayah 19 Location Makkah Number 96

ٱقۡرَأۡ بِٱسۡمِ رَبِّكَ ٱلَّذِی خَلَقَ ﴿1﴾

Werenga! (Iwe Mneneri (s.a.w), zomwe zikuvumbulutsidwa) mdzina la Mbuye wako Yemwe adalenga (zolengedwa zonse).[460]

خَلَقَ ٱلۡإِنسَـٰنَ مِنۡ عَلَقٍ ﴿2﴾

Adalenga munthu kuchokera ku magazi owundana.[461]

ٱقۡرَأۡ وَرَبُّكَ ٱلۡأَكۡرَمُ ﴿3﴾

Werenga! Ndipo Mbuye wako ndi Wopereka kwambiri.[462]

ٱلَّذِی عَلَّمَ بِٱلۡقَلَمِ ﴿4﴾

Yemwe waphunzitsa (munthu kulemba) ndi cholembera.

عَلَّمَ ٱلۡإِنسَـٰنَ مَا لَمۡ یَعۡلَمۡ ﴿5﴾

Waphunzitsa munthu zinthu (zambiri) zomwe (iye) sadali kuzidziwa.

كَلَّاۤ إِنَّ ٱلۡإِنسَـٰنَ لَیَطۡغَىٰۤ ﴿6﴾

Zoona ndithu koma munthu akupyola malire (podzikweza).

أَن رَّءَاهُ ٱسۡتَغۡنَىٰۤ ﴿7﴾

Chifukwa chodziona kuti walemera.

إِنَّ إِلَىٰ رَبِّكَ ٱلرُّجۡعَىٰۤ ﴿8﴾

Palibe chikaiko, (iwe Mneneri (s.a.w) kobwerera (onse) nkwa Mbuye wako basi; (adzawaukitsa).[463]

أَرَءَیۡتَ ٱلَّذِی یَنۡهَىٰ ﴿9﴾

Kodi wamuona yemwe akuletsa,

عَبۡدًا إِذَا صَلَّىٰۤ ﴿10﴾

Kapolo (wa Allah) akamapemphera?

أَرَءَیۡتَ إِن كَانَ عَلَى ٱلۡهُدَىٰۤ ﴿11﴾

Tandiuza ngati ali pachiongoko?

أَوۡ أَمَرَ بِٱلتَّقۡوَىٰۤ ﴿12﴾

Kapena kuti akulamulira zoopa Allah?

أَرَءَیۡتَ إِن كَذَّبَ وَتَوَلَّىٰۤ ﴿13﴾

Tandiuza (za woletsayo) ngati akutsutsa (zimene wadza nazo Mneneri) ndikunyoza (chikhulupiliro ndi ntchito yabwino)?

أَلَمۡ یَعۡلَم بِأَنَّ ٱللَّهَ یَرَىٰ ﴿14﴾

Kodi sakudziwa kuti Allah akuona (machitidwe ake. Ndipo adzamlipira)?

كَلَّا لَىِٕن لَّمۡ یَنتَهِ لَنَسۡفَعَۢا بِٱلنَّاصِیَةِ ﴿15﴾

Ayi ndithu ngati sasiya timukoka tsitsi lapatsumba (tiligwira mwamphamvu tsumba lake ndikukamponya ku Moto).

نَاصِیَةࣲ كَـٰذِبَةٍ خَاطِئَةࣲ ﴿16﴾

Tsumba labodza (ndiponso) lamachimo.

فَلۡیَدۡعُ نَادِیَهُۥ ﴿17﴾

Basi aliitane gulu lakelo, (la amene amakhala nawo pabwalo kuti amthandize pano pa dziko kapena tsiku lachimaliziro),

سَنَدۡعُ ٱلزَّبَانِیَةَ ﴿18﴾

Nafe tiitana azabaniya (angelo a ku Moto).

كَلَّا لَا تُطِعۡهُ وَٱسۡجُدۡ وَٱقۡتَرِب ۩ ﴿19﴾

Ayi ndithu usamumvere (pa zimene akukuletsazo); koma gwetsa nkhope yako pansi, ndipo dziyandikitse kwa Mbuye wako.