Settings
Surah The earthquake [Al-Zalzala] in Chewa
إِذَا زُلْزِلَتِ ٱلْأَرْضُ زِلْزَالَهَا ﴿1﴾
Likadzagwedezedwa dziko lapansi kugwedezeka kwake kwamphamvu,
وَأَخْرَجَتِ ٱلْأَرْضُ أَثْقَالَهَا ﴿2﴾
Ndipo nthaka idzatulutsa mitolo yake (zinthu zomwe zidali mkati mwake, monga akufa ndi miyala ya mtengo wapatali),
وَقَالَ ٱلْإِنسَٰنُ مَا لَهَا ﴿3﴾
Ndipo munthu adzanena (mwa mantha, ndikudabwa nthawi imeneyo). Ha! Yatani nthaka, (kodi Qiyâma yafika)?
يَوْمَئِذٍۢ تُحَدِّثُ أَخْبَارَهَا ﴿4﴾
Tsiku limenelo idzanena nkhani zake zonse, (zabwino kapena zoipa).[470]
بِأَنَّ رَبَّكَ أَوْحَىٰ لَهَا ﴿5﴾
Pakuti Mbuye wako adzailamula kutero (kuti igwedezeke ndikunena zimene zinkachitika pamwamba pake).
يَوْمَئِذٍۢ يَصْدُرُ ٱلنَّاسُ أَشْتَاتًۭا لِّيُرَوْا۟ أَعْمَٰلَهُمْ ﴿6﴾
Tsiku limenelo anthu adzachoka (m’manda) ali m’magulu obalalika kuti akasonyezedwe ntchito zawo (ndikudziwa chiwerengero chawo chimene chili kwa Allah).
فَمَن يَعْمَلْ مِثْقَالَ ذَرَّةٍ خَيْرًۭا يَرَهُۥ ﴿7﴾
Choncho, amene angachite chabwino cholemera ngati kanjere kakang’ono, adzaona malipiro ake.[471]
وَمَن يَعْمَلْ مِثْقَالَ ذَرَّةٍۢ شَرًّۭا يَرَهُۥ ﴿8﴾
Ndipo amene angachite choipa cholemera ngati kanjere kakang’ono, adzaona malipiro ake. (Allah sachitira chinyengo aliyense).